Wednesday, April 24, 2024

Featured Video

Latest Stories

Top 10 Music

Upcoming Events

Zomba City Festival

Fri, 26 Apr 2024 10:00:00 UTC @ Botanic Garden - 2024 Zomba City Festival is schedulled to take place on 26 to 28 April at Botanic Garden in Zomba This is a festival for all ages in the historic mountain city of Zomba. Celebrate Cultu... More Info
Queens Club Shut Down

Fri, 26 Apr 2024 19:00:00 UTC @ Queens Club - Queens Club Presents "Queens Club Shut Down" with music performances by Kelly Kay, Charisma, Teddy Makadi and Praise Umali. The show will take place at Queens Club in Mzuzu on 26 April... More Info

Apolisi akwidzinga msing`anga pogona ndi mtsikana wa chichepere

A police ku Mzuzu akusungira m`chitokosi msing`anga wa zaka makumi awiri ndi zisanu pa mulandu ogona ndi msungwana wa zaka khumi ndi zitatu.

Msing`angayi ndi Charles Muwa yemwe amachokera m`mudzi mwa Kulola mfumu yaikulu Mkanda M`boma la Mulanje.

Wachiwiri kwa M`neneri wa apolisi ku Mzuzu, Cecilia Mfune wati msungwanayi anachoka ku Ekwendeni loweruka komwe amakhala ndi agogo ake kupita ku Chibavi kwa mayi ake.

Ali ku Chibavi, anapezeka wasowa kotero mayi ake anadziwitsa anthu ozungulira za nkhaniyi.

“Atafufuzidwa komwe ali, anapezeka kunyumba ya msing`angayi yemwe amakhalaso m`mudzi omwewo,” malingana ndi a Mfune.

Msungwanayu anaulura kuti anagona kunyumba kwa msing`angayi komweso anamuchita zadama.

Bambo Muwa akuyembekezeka kukaonekera ku bwalo la milandu komwe  akayankhe mulandu ogona ndi mwana wachichepere.

Subscribe to our Youtube Channel:

Related Posts

LEAVE A REPLY

Please enter your comment!
Please enter your name here

Popular Articles