Thursday, March 28, 2024

Featured Video

Top 5 This Week

Top 10 Music

[showmfm]

Upcoming Events

[showevents]

Bambo Wansanje Abaya Mzake Chifukwa Cha Mkazi Wake Wakale

Polisi ya kanengo ku Lilongwe ikusungira mchitokosi mzim`bambo wa zaka makumi awiri ndi zitatu (23) pa mlandu wokupha mzim`bambo nzake wa zaka makumi atatu ndi zisanu (35) kamba ka mkazi.

Wachiwiri kwa ofalitsa nkhani pa polisi ya kanengo, Esther Mkwanda wati mzim`bamboyu yemwe dzina lake ndi Gift Sitina anabaya a Austin Chirombo lachinayi lapitali m`mudzi mwa Mchezi mdera la mfumu yaikulu Chimutu ku Lilongwe.

Malinga ndi a Mkwanda, Sitina anali pa banja ndi Mkazi wa malemuwa koma kamba ka nkhani zina banjalo linatha.

Ngakhale a Sitina akhala akuchondelera Mzimayiyo kuti abwelerane, palibe cha phindu chilichonse chomwe kuchondelera kwao kunaphula.

“Mosapanganika, zinachitika kuti a Sitina anayandikana ndi nyumba yomwe mkazi wawo wakaleyo amakhala ndi mwamuna watsopanoyo, malemu Chirombo. Chikondi cha anthu awiriwa chinafika pokoma mpaka a bambo Sitina anayamba kupanga nsanje,” anafotokoza a Mkwanda.

Pa tsikulo, bambo Sitina adapita kunyumba kwa a Chirombo atanyamula mpeni m`manja omwe anagwiritsa ntchito pobayira bambo mzawoyo.

Mwatsoka a Chirombo anamwalira akufika ku chipatala cha Daeyang Luke. Zotsatira za ku chipatala zidaonetsa kuti malemu Chirombo adamwalira kamba kotaya magazi ambiri.

A Sitina amachokera m`mudzi mwa Dzuwa Mdera la mfumu yaikulu Mchiramwera ku Lilongwe ndipo akuyembekezeka kukaonekera ku bwalo la milandu komwe akayankhe mlandu okupha munthu omwe umatsutsana ndi gawo 209 la dziko lino.

Related Posts

LEAVE A REPLY

Please enter your comment!
Please enter your name here

Popular Articles