Thursday, April 25, 2024

Featured Video

Latest Stories

Top 10 Music

Upcoming Events

Zomba City Festival

Fri, 26 Apr 2024 10:00:00 UTC @ Botanic Garden - 2024 Zomba City Festival is schedulled to take place on 26 to 28 April at Botanic Garden in Zomba This is a festival for all ages in the historic mountain city of Zomba. Celebrate Cultu... More Info
Queens Club Shut Down

Fri, 26 Apr 2024 19:00:00 UTC @ Queens Club - Queens Club Presents "Queens Club Shut Down" with music performances by Kelly Kay, Charisma, Teddy Makadi and Praise Umali. The show will take place at Queens Club in Mzuzu on 26 April... More Info

Achinyamata Atonyokenso Ndi “Midori”

Patangotha miyezi ingapo chiletseleni mowa wotchipa wa midori omweso ena amati mkalabongo, Bungwe loona ndi kuyeza mulingo wa katundu la Malawi Bureau of Standards (MBS) latchotsa chiletso chake chomwe linayika pa mowawu kuti usapezekenso pa msika.

mowa wotchipa wa Midori

Mosakayikira ndi kuchotsera, achinyamata ku Malawi kuno atonyokaso mu 2018.

Bungwe la MBS lauza ma kampani omwe amapanga mowawu tsopano kuti ayambe kuika mowawu m`mabotolo a galasi osati m`mene amauyikira m`ma botolo a pulasitiki kalero.

Koma ngakhale izi zilichoncho, bungwe lina lomwe limaona za ufulu wa ogula katundu la Consumers Association of Malawi (CAMA), lati ganizoli silabwino pakuti muyezo wa zinthu zina zomwe zimaikidwa m`mowawu siunasinthe.

“Chomwe chasinthidwa m`mowawu ndi botolo chabe koma osati muyezo ndi mulingo wa zinthu zina zomwe zimaikidwa m`mowawu,” watero mkulu wa bungwe la CAMA, a John Kapito.

A Kapito apitiriza kuti izi zingopititsa patsogolo mchitidwe wa kumwa mowa mwa uchidakwa pakati pa achinyamata poti ndiwo amakonda mowawu chifukwa ndi wotchipa.

Chaka chatha, bungwe la MBS linalanda mowawu potsatira dandaulo lomwe anthu ndi mabungwe ena okhuzidwa anapereka za mowawu.

Subscribe to our Youtube Channel:

Related Posts

LEAVE A REPLY

Please enter your comment!
Please enter your name here

Popular Articles