Friday, April 26, 2024

Featured Video

Latest Stories

Top 10 Music

Upcoming Events

Zomba City Festival

Fri, 26 Apr 2024 10:00:00 UTC @ Botanic Garden - 2024 Zomba City Festival is schedulled to take place on 26 to 28 April at Botanic Garden in Zomba This is a festival for all ages in the historic mountain city of Zomba. Celebrate Cultu... More Info
Njuchi Day

Sat, 27 Apr 2024 10:00:00 UTC @ New Village House (Kampala Manase) - Elinationa And No Limit Presents Njuchi Day Music show with Njuchi Zitatu. The show will take place at New Village House in Manase on 27 April 2024 and it will have music performances b... More Info

Wodwala Misala Apezeka Ali Mu Unifolomu Ya Apolisi

Mzibambo wazaka makumi awiri ndi zitatu yemwe akuganiziridwa kuti ndi wodwala nthenda ya misala wakwidzingwidwa ndi apolisi atapezeka atavala unifolomu ya apolisi pa msewu.

Malingana ndi Mneneri wa apolisi ya Kanengo Laban Mkalani, mzibamboyu yemwe dzina lake ndi Alim Amin ananjatidwa m’mawa wa lachitatu pa 4 Malichi.

A Makalani ati Amini adamangwidwa ndi apolisi omwe amalondera pa tsikulo. Akuti Mzibamboyu anakwidzingidwa munsewu wa thala wa Chendawaka akuimitsa magalimoto ngati ndi wa polisi wa pa msewu.

Chodabwitsa chinali chokuti, ngakhale anatchena bwinobwino zovala za apolisi komaso chipewa, ku mapazi ake anali asanavale kalikonse.

Pakadali pano, munthuyu akusungidwa pa polisi ya Kanengo pamene apolisi akupanga kafukufuku oti adziwe ngatidi ali wamisala komaso komwe anatenga yunifolomu ya apolisi.

Amin amachokera mdera la Mfumu yaikulu Kabudula ku Lilongwe.

 

Subscribe to our Youtube Channel:

Related Posts

LEAVE A REPLY

Please enter your comment!
Please enter your name here

Popular Articles