Thursday, March 28, 2024

Featured Video

Top 5 This Week

Top 10 Music

[showmfm]

Upcoming Events

[showevents]

Kathyali Wina Wanjatidwa kamba kokuba Katundu wa K2 millioni

Apolisi mtowinshipi ya Limbe ku Blantyre anjata kathyali wina kamba kukoba katundu okwana ndalama k2.2 million ndipo mkuyuyu dzina lake ndi Blessings Mtitule.

M’neneri wa polisi wa ku Limbe  Widson Nhlane wanena kuti analandila uthenga ku Chokera kwa anthu okhala ku Chinyonga pa 18 July, 2018 kuti mbava zathyola nyumba ya Mai wina ndipo zinaba makina akomputa, iphone, masipika komaso nsapato zachizibambo zokwana 12 ndi zovala zokwana k2,240,000.

Apolisi atapanga chipikisheni pa 23, Mtitule ananjatidwa ndipo anamupeza ndi katundu yemwe wa tchulidwayi.

Mneneri wa polisiyu wanena kuti adakali kalikiliki kufufuza kandundu otsala yemwe adabebwayo.

Pakadali pano apolisi amema anthu amderali kuti asanyozere kutsina khutu apolisi pankhani ya zimbalangondozi akaziona.

Mtitule amakhala m’mudzi mwa Mtalala, mfumu yaikule Nsomba ku Blantyre ndipo akuyembekera kukalowa Court sabata la mawa.

Related Posts

Face of Malawi
Face of Malawihttps://www.faceofmalawi.com
For more Info: info@faceofmalawi.com

LEAVE A REPLY

Please enter your comment!
Please enter your name here

Popular Articles