Wednesday, April 24, 2024

Featured Video

Latest Stories

Top 10 Music

Upcoming Events

Zomba City Festival

Fri, 26 Apr 2024 10:00:00 UTC @ Botanic Garden - 2024 Zomba City Festival is schedulled to take place on 26 to 28 April at Botanic Garden in Zomba This is a festival for all ages in the historic mountain city of Zomba. Celebrate Cultu... More Info
Queens Club Shut Down

Fri, 26 Apr 2024 19:00:00 UTC @ Queens Club - Queens Club Presents "Queens Club Shut Down" with music performances by Kelly Kay, Charisma, Teddy Makadi and Praise Umali. The show will take place at Queens Club in Mzuzu on 26 April... More Info

M’kango Olusa Wavulaza Anthu Atatu M’boma La Chitipa

Mkango olusa wavulaza anthu atatu m’boma la Chitipa pomwe amafuna kupha mkangowo.

Izi zachitika m’mudzi wa Kasisi pomwe anthu atatuwa amafuna kupha m’kangowu ndi mikondo komanso mkhwangwa, koma m’kanguwo unakwanitsa kuluma anthuwa kenako m’kuthawa.

Anthu ovulalawa akudziwika ndi maina awa Mabacha Sibale, Kauka komanso Haonga omwe amakhala m’mudzi momwemo.

Lion-Malawi

Mkango wavulaza anthu atatu

Anthu atatuwa awatengela ku chipatala Cha Kameme zinthuzi zitango chitika.

Pakadali pano apolisi anenakuti m’kangowu udakali kuyenda mu dera la Kasisi ndipo apeleka chenjezo kwa anthu am’derali kuti ankhale mosamala chifukwa cha mkangowu.

M’mawa wa lachinayi, Mneneli wa Polisi ku chitipa Gladwell Simwaka adanena kuti m’kangowo wakhala ukuvutitsa m’madera amfumu yaikulu Kameme T/A Mwaulambia m’boma la Chitipa.

Ndipo adaonjezera ponena kuti mkangowu akuwukaikira kuti wathawa ku malo osunga zinyama ku Luangwa mdziko la Zambia.

Mkangowu  wapha Ng’ombe zisanu ndi imodzi m’mudzi mwa Kasisi.

Pakadali pano apolisi ndi anthu oyang’anila zinyama akusaka saka mkangowu. Simwaka watero.

Subscribe to our Youtube Channel:

Related Posts

Face of Malawi
Face of Malawihttps://www.faceofmalawi.com
For more Info: info@faceofmalawi.com

Popular Articles