Friday, April 19, 2024

Featured Video

Latest Stories

Top 10 Music

Upcoming Events

Zomba City Festival

Fri, 26 Apr 2024 10:00:00 UTC @ Botanic Garden - 2024 Zomba City Festival is schedulled to take place on 26 to 28 April at Botanic Garden in Zomba This is a festival for all ages in the historic mountain city of Zomba. Celebrate Cultu... More Info
Njuchi Day

Sat, 27 Apr 2024 10:00:00 UTC @ New Village House (Kampala Manase) - Elinationa And No Limit Presents Njuchi Day Music show with Njuchi Zitatu. The show will take place at New Village House in Manase on 27 April 2024 and it will have music performances b... More Info

A Mutharika ndi A Chilima Akumana Maso ndi Maso Mu Sepitembala

Pali kuthekera kwakulu kuti mtsogoleri wa dziko lino, Dr Peter Mutharika komaso wachiwiri wawo, Dr Saulos Chilima – azitsogoleri awiri omwe pakadali pano ali ngati mphaka ndi khoswe pa ndale atha kukumana pa 1 sepitembala ku mwambo wa a Ngoni ku Ntcheu.

Mfumu ya angoni, Inkosi ya Makosi Gomani V yaitanitsa azitsogoleri awiriwa kuti azakhale nawo pa mwambowu omwe utazachitikire m’mudzi mwa Nkolimbo, mdera la mfumu yaikulu kwataine mboma la Ntcheu.

chithuzi chakale cha atsogoleri awiriwa

Malinga ndi chikalata chochokera kwa mfumu ya angoniyi, mtsogoleri wa dziko lino waitanidwa kuzakhala mlendo olemekezeka pa mwambowu komaso a Chilima omwe aitanidwa kuzapezeka pa mwambowu monga iwoso ndi amtundu wa chingoni.

Mwambowu omwe umatchedwa Umhlangano umachitika chaka chilichonse ndi cholinga chopititsa patsogolo chikhalidwe cha mtundu wa chi Ngoni.

Chaka chino, mwambowu uyamba pa 31 mwezi uno kumalizira pa 1 sepitembala.

Malinga ndi malamulo, mtsogoleri wa dziko ndi wachiwiri wake amayembekezeka kupasana chanza pa mwambo kapena msonkhano ulionse omwe awiriwa apezeka.

A Chilima akhala akupangisa misonkhano yawo limodzi ndi gulu la ndale lawo la United Transformation Movement (UTM) atatuluka chipani cholamula cha Democratic Progressive Party (DPP) chomwe mtsogoleri wake ndi a Mutharika.

Chitulukireni a Chilima mu DPP, azitsogoleri awiriwa akhala asakuonana ndi diso labwino monga m’mene zimakhalira khoswe ndi mphaka.

 

Subscribe to our Youtube Channel:

Related Posts

LEAVE A REPLY

Please enter your comment!
Please enter your name here

Popular Articles