Tuesday, April 23, 2024

Featured Video

Latest Stories

Top 10 Music

Upcoming Events

Zomba City Festival

Fri, 26 Apr 2024 10:00:00 UTC @ Botanic Garden - 2024 Zomba City Festival is schedulled to take place on 26 to 28 April at Botanic Garden in Zomba This is a festival for all ages in the historic mountain city of Zomba. Celebrate Cultu... More Info
Queens Club Shut Down

Fri, 26 Apr 2024 19:00:00 UTC @ Queens Club - Queens Club Presents "Queens Club Shut Down" with music performances by Kelly Kay, Charisma, Teddy Makadi and Praise Umali. The show will take place at Queens Club in Mzuzu on 26 April... More Info

Nyamata Wazaka 18 Wamwalira Kamba Ka Nyama Ya ‘Eid’ Ku Mulanje

Nyamata wazaka 18 yemwe amadziwika ndi dzina la Patrick Salimu wamwalira ku Mulanje kamba ka ndewu yomwe inabuka chifukwa cha nyama yomwe inaphedwa pa msonkhano wa chipembezo cha chisilamu wa Eid-Al-Adha.

M’bale wa omwalirayu, Sitolo Mathewe anauza apolisi kuti lachitatu lapitali, Patrick anapita ku Msonkhano wa Eid komwe anakapatsidwa nyama yoti akadyere pakhomo.

Malinga ndi m’neneri wa apolisi ku Mulanje, Greshiam Ngwira, Patrick atafika ndi nyamayo kunyumba, munthu wina anaonetsa chidwi chofuna kugula nyamayo koma malemuwa anakaniza kupanga malonda ndi munthuyo.

Mwadzidzi, munthuyo yemwe dzina lake ndi Steve Kathala anasomphola nyamayo ndi kutulutsa K200 yomwe anpereka kwa malemuwa ngati malipiro pa nyamayo, koma posakhalitsa ndewu inabuka pakati pa awiriwa.

“Pomaliza pa ndewu malemuwa anapwetekedwa kwambiri moti anthu akufuna kwabwino anawatengere ku chipatala chachikulu m’bomali komwe adamwalira mwadzidzi akufika kumene.,”adatero a Ngwira.

Pakadali pano, apolisi akusakasaka a Steve Kathala kuti akayankhe mulandu okupha munthu akapezeka olakwa mu bwalo la milandu.

Patrick anali wa m’mudzi mwa Mpholiwa mdera la mfumu yaikulu Njema ku Mulanje.

 

 

Subscribe to our Youtube Channel:

Related Posts

LEAVE A REPLY

Please enter your comment!
Please enter your name here

Popular Articles