Thursday, April 18, 2024

Featured Video

Latest Stories

Top 10 Music

Upcoming Events

Zomba City Festival

Fri, 26 Apr 2024 10:00:00 UTC @ Botanic Garden - 2024 Zomba City Festival is schedulled to take place on 26 to 28 April at Botanic Garden in Zomba This is a festival for all ages in the historic mountain city of Zomba. Celebrate Cultu... More Info
Njuchi Day

Sat, 27 Apr 2024 10:00:00 UTC @ New Village House (Kampala Manase) - Elinationa And No Limit Presents Njuchi Day Music show with Njuchi Zitatu. The show will take place at New Village House in Manase on 27 April 2024 and it will have music performances b... More Info

A Ben Phiri Ati Maliseche Athu ndi Peter Mutharika

Mkulu oyang’anira za chisankho ku chipani cholamula cha Democratic Progressive Party (DPP), a Ben Phiri auza anthu kuti mtsogoleri wadziko lino Peter Muntharika ndi Maliseche awo.

a Ben Phiri pa msonkhano

A Ben Phiri ayankhula mawuwa ku msonkhano wa chipani cholamulachi ku Zomba omwe cholinga chake unali kumema anthu kuti akalembetse mavoti kuti azasankhe a Peter Mutharika.

M’mau awo, a Phiri anayerekeza a Peter Mutharika ndi maliseche ponena kuti munthu umabisa maliseche ako choncho anthu aku Zomba akuyenera kukavotera a Peter Mutharika pa zisankho za 2019.

“Maliseche munthu umabisa ako. Ife wathu kum’mwera kuno ndo professor Peter Mutharika basi. Maliseche athu ndi amenewo,” anatero a Phiri.

Koma anthu ena adzudzula a Ben Phiri ponena kuti sadasakhe mawu abwino omuyerekezera mtsogoleri wa dziko linoyu.

Kanema yemwe akuonetsa a Phiri akukamba izi wafala pa tsamba la intaneti la facebook komanso whatsapp.

Subscribe to our Youtube Channel:

Related Posts

LEAVE A REPLY

Please enter your comment!
Please enter your name here

Popular Articles