Thursday, March 28, 2024

Featured Video

Top 5 This Week

Top 10 Music

[showmfm]

Upcoming Events

[showevents]

Mkulu wina wadzinjata M’boma la Mzimba

Mkulu wina wa zaka 63 wadzinjata m’boma la Mzimba.

Mkuluyi amadziwika ndi dzina loti Davison Kumwenda ndipo amakhala m’dela la Mfumu yaikulu M’mbelwa ku Mzimba.

M’neneri wa polisi Peter Botha wanena kuti Kumwenda anachoka kunyumba kwake osatsanzika anthu apakhoma lake.

Ndipo masana wake bambo Kumwenda adawapeza atadzinjata mu mtengo wamango pafupi ndi nyumba yawo.

Botha adaonjezera ponena kuti Kumwena anali pa mkangano wa malo ndi anthu apachibale ndipo amfumu am’mudzimo amayendetsa nkhani ya malo.

Imfa ya bambo kumwenda yachitika patangotha masiku ochepa pomwe bambo wina wazaka 45 Josted Saka atadzinjataso m’boma la Mzimba.

 

 

Related Posts

Face of Malawi
Face of Malawihttps://www.faceofmalawi.com
For more Info: info@faceofmalawi.com

LEAVE A REPLY

Please enter your comment!
Please enter your name here

Popular Articles