Thursday, March 28, 2024

Featured Video

Top 5 This Week

Top 10 Music

[showmfm]

Upcoming Events

[showevents]

Apolisi Anjata Mkulu wina Kamba Kopha Gule Wamkulu Ku Kasungu

Apolisi anjata Mkulu wina wa zaka 23 ku Kasungu kamba kupha Gule wa mkulu (Chilombo), ndipo mkuluyi akudziwika ndi dzina loti McCloud Mtonga.

Mtonga adakumana ndi Guleyu  pa 11 December, 2018, ndipo Guleyu adayamba kuthamangitsa Mtonga motsatizana ndikukwapulidwa kwambiri.

Atatopa Mtonga analanda ndodo ya Guleyo, m’kuyamba kuchibwezera kwa Guleyo.

Mpaka Guleyo adagwa pansi, atapita naye Guleyo ku Chipatala,  madotolo analegeza kuti Guleyo wamwalira.

Gule wa Mkuluyi amadziwika ndi dzina loti Ganizani Soko ndipo izi zidachitika m’mudzi wa Chifisi, sub/TA Mnyanja ku Kasungu.

Pakadali pano McCloud Mtonga ali m’manja mwa apolisi.

Related Posts

Face of Malawi
Face of Malawihttps://www.faceofmalawi.com
For more Info: info@faceofmalawi.com

LEAVE A REPLY

Please enter your comment!
Please enter your name here

Popular Articles