Thursday, April 25, 2024

Featured Video

Latest Stories

Top 10 Music

Upcoming Events

Zomba City Festival

Fri, 26 Apr 2024 10:00:00 UTC @ Botanic Garden - 2024 Zomba City Festival is schedulled to take place on 26 to 28 April at Botanic Garden in Zomba This is a festival for all ages in the historic mountain city of Zomba. Celebrate Cultu... More Info
Queens Club Shut Down

Fri, 26 Apr 2024 19:00:00 UTC @ Queens Club - Queens Club Presents "Queens Club Shut Down" with music performances by Kelly Kay, Charisma, Teddy Makadi and Praise Umali. The show will take place at Queens Club in Mzuzu on 26 April... More Info

Mkulu wina wamangidwa Miyezi 30 kamba koba Ng’ombe M’boma la Chikwawa

Bwalo la milandu la Makande ku Chikwawa lalamula bambo Mexon Chaleka azaka 48 kuti akakhale kundende zaka ziwiri ndi miyezi isanu ndi umodzi (6) kaamba koba ng’ombe ziwiri.

Chaleka anapalamula mulanduwu usiku wapa 31 October, 2018 m’mudzi wa Gonyo kwa Ngabu. Usikuwo, Chaleka anali ndi anzake ena awiri ndipo adafika pa khola la Mayi Lucy Kanthema.

“Panthawiyo, Maiwa adali akugona mkhonde la nyumba yawo, ndipo anaona anthu ena atatu akulunjika kukhola lawo.

Atalondola anthu okayikitsawo, mwini khola uja anapeza kuti kholalo ndi losegula ndipo ng’ombe ziwiri mulibe.

Kenako adaona anthu okuba aja chapafupi ndipo adakuwa, zomwe zidapangisa mbava zija kuthawa.

Koma anthu am’mudzimo anazuka mwachangu ndikugwira a Mexon Chaleka.” Constable Foster Benjamin adatero polankhula ndi atolankhani.

Apa, a Chaleka anawalondolera anthu aja komwe anabisa zifuyo zija.

Chaleka anatengeredwa ku polisi ya Ngabu komwe anamusegulira mulandu okuba ng’ombe.

Koma mulandu andaukana pa khoti, ndipo a boma kudzera kwa Constable Mwanyala Goche adabweresa mboni zinayi.

Abomawa anapempha bwalo kuti lipereke chilango chokhwima kwa ozengedwa mulanduwo maka poganiza ndi kabwerebwere ku ndende.

Mu chaka cha 2015, Chaleka anapasidwanso chilango ngati chomwecho pa mulandu okuba mbuzi.

Ndipo popereka chigamulo, oweruza milandu kubwaloli, a Chiyembekezo Phiri anagwirizana ndi maganizo a boma ndipo anadandaula mchitidwe okuba zifuyo omwe anati wakula kwambiri m’boma la Chikwawa.

A Phiri apeza Chaleka kuti ndiolakwa ndipo analamula kuti akakhale kundende miyezi 30 komwe akagwire ukaidi wakalavula gaga.

Chaleka amachokera mmudzi wa Kachipepa m’dera lamfumu yaikulu Ngabu m’boma la Chikwawa.

Subscribe to our Youtube Channel:

Related Posts

Face of Malawi
Face of Malawihttps://www.faceofmalawi.com
For more Info: info@faceofmalawi.com

LEAVE A REPLY

Please enter your comment!
Please enter your name here

Popular Articles