Mbava Zaba M’kachisi Ku Zambia

Mbava Zaba M’kachisi Ku Zambia

Published on July 4, 2019 at 11:27 AM by Face of Malawi

78 words • approx. 1 min read

Mbava zosadziwika bwino zathyola kachisi ya  Kansuswa Seveth-Day Adventist mudera la Mufulira ku Zambia ndipo mbavazo zaba zipangizo zogwilitsa ntchito popemphera ndi katundu wina okwana k2, 700.

Malingana ndi malipoti ochokera kwa akulu am’pingo awuza atolankhani kuti mbavazo zidathyola kachisilo pausiku walachiwiri, ndipo adapitiriza kunena kuti Mbavazo zathawa ndi katundu osiyanasiyana wa Tchalitchilo.

Munthu ongodutsa ndiyemwe odawona izi ndipo adathamangila kukawuza akulu ampingo omwe amakhala pafupi ndi kachisilo.

Akulu ampingo adakapereka lipoti kupolice ndipo apolisi  ali kalikiliki kusaka mbavazo

Subscribe to our Youtube Channel: