Wednesday, April 24, 2024

Featured Video

Latest Stories

Top 10 Music

Upcoming Events

Zomba City Festival

Fri, 26 Apr 2024 10:00:00 UTC @ Botanic Garden - 2024 Zomba City Festival is schedulled to take place on 26 to 28 April at Botanic Garden in Zomba This is a festival for all ages in the historic mountain city of Zomba. Celebrate Cultu... More Info
Queens Club Shut Down

Fri, 26 Apr 2024 19:00:00 UTC @ Queens Club - Queens Club Presents "Queens Club Shut Down" with music performances by Kelly Kay, Charisma, Teddy Makadi and Praise Umali. The show will take place at Queens Club in Mzuzu on 26 April... More Info

Adula Madzi Kusukulu ya Anthu Osaona

Bungwe loona za madzi mchigawo chaku mpoto la Northern Region Water Board (NRWB) ladula madzi ku sukulu ya anthu osaona ya Ekwendeni School fo the Blind m’boma la Mzimba kamba ka ngongole yosachepera 1.5 milion kwacha yomwe sukuluyi ilinayo ku bungweli.

Frances Mkandawire yemwe ndi mphunzitsi wamkulu pa sukuluyi wati ngongoleyi yakhala koposera miyezi iwiri.

A Mkandawire anapitiliza kunena kuti vutoli lakhudza kwambili nkhani ya ukhondo pa sukuluyi.

Iwo anapitiliza kuti akulephera kulipira ngongoleyi kamba koti sukuluyi imayendera thandizo lomwe limalandira yomwe ndi 450, 000 kwacha pa mwezi, zomwe nkunena kwawo sizokwanira kuti ithetse mavuto omwe amakumana nawo.

“Kusowa kwa zipangizo ndiye vuto lomwe tikukumana nalo, ndalama yomwe timapatsiwa pa mwezi ndi 450, 000 kwacha yomwe siyokwanira kuti tigwiritse ntchito pa zofunikira za pasukuluyi, kuchokera pandalamayi timayenera tigule chakudya, zipangizo zokhudza ndi maphunziro, kulipira ngongele komaso malipiro a anthu ogwira ntchito zomwe sizinthu zophweka,” anatero a Mkandawire.

A Mkandawire anati akulu akulu a sukuluyi akhala akugundana mitu pofuna kuthetsa vutoli koma szikuthandiza.

Poyankhulapo ofalitsa nkhani ku bungwe loona za madzi mchigawochi a Edward Nyirenda anati kudula madzi ndiye inali njira yokhayo anali nayo poti zokambirana zinalephereka.

“Kukambirana ndi imodzi mwa njira zathu, tinayesera kukumana ndi akuluakulu a sukuluyi koma sizinapindule kanthu. Sukuluyi ili ndi magawo awiri tinadula gawo limodzi kuyembekezra kuti abwera poyera ndikulipira koma mmalo mwake anakumba mjigo zomwe ndikuphwanya chipangano,” anatero a Nyirenda.

Mmbuyomu unduna oona za maphunziro mdziko muno atafunsidwa zokhudzana ndi chithandizo cha anthu ofunika chithandizo chapadera mmasukulu, nneneri wa undunawu a Lindiwe Chide anati boma likugwirzana ndi anthu akufuna kwabwino kuti athandizepo m’malo ngati amenewa.

Subscribe to our Youtube Channel:

Related Posts

Flora Mitumba
Flora Mitumba
Email: info@faceofmalawi.com

LEAVE A REPLY

Please enter your comment!
Please enter your name here

Popular Articles