Wednesday, May 1, 2024

Featured Video

Latest Stories

Top 10 Music

[showmfm]

Upcoming Events

[showevents]

A Ben Phiri Ati Maliseche Athu ndi Peter Mutharika

Mkulu oyang’anira za chisankho ku chipani cholamula cha Democratic Progressive Party (DPP), a Ben Phiri auza anthu kuti mtsogoleri wadziko lino Peter Muntharika ndi Maliseche awo.

a Ben Phiri pa msonkhano

A Ben Phiri ayankhula mawuwa ku msonkhano wa chipani cholamulachi ku Zomba omwe cholinga chake unali kumema anthu kuti akalembetse mavoti kuti azasankhe a Peter Mutharika.

M’mau awo, a Phiri anayerekeza a Peter Mutharika ndi maliseche ponena kuti munthu umabisa maliseche ako choncho anthu aku Zomba akuyenera kukavotera a Peter Mutharika pa zisankho za 2019.

“Maliseche munthu umabisa ako. Ife wathu kum’mwera kuno ndo professor Peter Mutharika basi. Maliseche athu ndi amenewo,” anatero a Phiri.

Koma anthu ena adzudzula a Ben Phiri ponena kuti sadasakhe mawu abwino omuyerekezera mtsogoleri wa dziko linoyu.

Kanema yemwe akuonetsa a Phiri akukamba izi wafala pa tsamba la intaneti la facebook komanso whatsapp.

Related Posts

LEAVE A REPLY

Please enter your comment!
Please enter your name here

Popular Articles