Thursday, April 25, 2024

Featured Video

Latest Stories

Top 10 Music

Upcoming Events

Zomba City Festival

Fri, 26 Apr 2024 10:00:00 UTC @ Botanic Garden - 2024 Zomba City Festival is schedulled to take place on 26 to 28 April at Botanic Garden in Zomba This is a festival for all ages in the historic mountain city of Zomba. Celebrate Cultu... More Info
Queens Club Shut Down

Fri, 26 Apr 2024 19:00:00 UTC @ Queens Club - Queens Club Presents "Queens Club Shut Down" with music performances by Kelly Kay, Charisma, Teddy Makadi and Praise Umali. The show will take place at Queens Club in Mzuzu on 26 April... More Info

Gogo Waphedwa m’boma la Dowa

Apolisi m’boma la Dowa akusaka zimbalangondo zosadziwika zomwe zapha gogo wachizimayi wa zaka 94 zakubadwa m’mudzi mwa Chilomba, mfumu yaikulu Msakambewa.

Malingana ndi M’neneri wa polisi Sergeant Richard Mwakayoka Kaponda, adanena kuti malemuwa dzinalawo ndi Mai Talius Kwenda omwe adawapeza ataphedwa mudimba pa malo wena m’mudzi mwa Chilomba.

Powonjezera Akaponda adauza mtolankhani wathu kuti Mayi Kwenda amakhala m’mudzi mwa Chibanzi ndipo amakhala ndi chidzukulu chawo.

”Mayiwa adachoka pa khomo pawo pa 19 july,2018 m’kupita ku Lisongwe komwe kunali sadaka koma Mayiwa sadakafika kumaloko kenako ndi pamene anthu anawapeza ataphedwa mu dimba la bambo Laston Chivundula pa 21 july, 2018” Kaponda adatero.

Kenako Kaponda adaonjezera kunena kuti apolisi atafika pamalopo m’kupanga chipikisheni adaona kuti mayiwa anaphedwa ndi zipangizo zokutwa kwambiri.

Pakadali pano apolisi ali kalikiliki kufufuza anthu omwe adapha mayiwa ndipo apempha anthu am’deramo kuti awatsine khutu akanva zanthu adapha Mai Kwenda.

Subscribe to our Youtube Channel:

Related Posts

Face of Malawi
Face of Malawihttps://www.faceofmalawi.com
For more Info: info@faceofmalawi.com

LEAVE A REPLY

Please enter your comment!
Please enter your name here

Popular Articles