Thursday, April 25, 2024

Featured Video

Latest Stories

Top 10 Music

Upcoming Events

Zomba City Festival

Fri, 26 Apr 2024 10:00:00 UTC @ Botanic Garden - 2024 Zomba City Festival is schedulled to take place on 26 to 28 April at Botanic Garden in Zomba This is a festival for all ages in the historic mountain city of Zomba. Celebrate Cultu... More Info
Queens Club Shut Down

Fri, 26 Apr 2024 19:00:00 UTC @ Queens Club - Queens Club Presents "Queens Club Shut Down" with music performances by Kelly Kay, Charisma, Teddy Makadi and Praise Umali. The show will take place at Queens Club in Mzuzu on 26 April... More Info

Mphunzitsi wam’kulu Pa Sukulu ina wazipha kamba kopereka mimba kwa mwana wa Sukulu

Mphunzitsi wamkulu pa sukulu ina ya primary ku Nkhotakota wadzipha kamba kopereka mimba kwa mwana wa sukulu.

Mphunzitsiyu dzina lake ndi Mr. Darwin Nkhoma ndipo adali mphunzitsi wa sukulu ya Kaweluwelu m’boma la Nkhotakota.

Mneneri wa polisi m’bomali  Ignatius Esau wati Mphunzitsiya adayamba kupanga zachisembwere ndi mtsikana wa zaka khumi ndi zinayi ndipo adamupatsa mimba. Pakadali pano mtsikanayi ali ndi mimba ya miyezi itatu.

Nkhaniyi itanveka m’mudzimo anthu ena anatsina khutu anthu amabungwe monga a “Girl Child education, ndipo pa 27, july mkulu wa chimasomasoyu adayendeledwa ndi amabungwe pa khomo pake kenako adamutengera pa sukulu yomwe amayang’anila. izi zidachititsa theng’enenge mkuluyi.

Ndipo atadziwa kuti mabungwewa akatsina khutu apolisii, Nkhoma adanamiza m’kaziwake kuti akukayan’ganila mbuzi ngati zidali zotsekeledwa koma Nkhoma sadabwereleso nyumba.

Patapita masiku awiri, Nkhoma yemwe amachokera m’mudzi mwa Kamphandika m’fumu yayikulu Kafuzila m’derali adapezeka atazikhweza chapafupi ndi nkhalango ya m’mudzimo.

 

Subscribe to our Youtube Channel:

Related Posts

Face of Malawi
Face of Malawihttps://www.faceofmalawi.com
For more Info: info@faceofmalawi.com

LEAVE A REPLY

Please enter your comment!
Please enter your name here

Popular Articles