Wednesday, April 24, 2024

Featured Video

Latest Stories

Top 10 Music

Upcoming Events

Zomba City Festival

Fri, 26 Apr 2024 10:00:00 UTC @ Botanic Garden - 2024 Zomba City Festival is schedulled to take place on 26 to 28 April at Botanic Garden in Zomba This is a festival for all ages in the historic mountain city of Zomba. Celebrate Cultu... More Info
Queens Club Shut Down

Fri, 26 Apr 2024 19:00:00 UTC @ Queens Club - Queens Club Presents "Queens Club Shut Down" with music performances by Kelly Kay, Charisma, Teddy Makadi and Praise Umali. The show will take place at Queens Club in Mzuzu on 26 April... More Info

A Harry Mkandawire Aombola Mzimayi Opangidwa Chitaka ku Rumphi

Wachiwiri kaotsatira Mtsogoleri wa Chipani cha Malawi Congress (MCP), Harry Mkandawire waombola mzimayi yemwe anapangidwa chitaka ku Rumphi pomupatsa ndalama komaso kumugulira thumba la feteleza.

Malingana ndi mapikitchala komaso ma lipoti omwe anapezeka pa tsamba la intaneti la fecebook, Mzimayiyu anali ndi ndalama zokwana K18,000 zomwe anapita nazo ku msika wina ku Rumphi kuti akagule feteleza.

Koma asanagule feteleza, mayiwa anayamba wagula zakudya zina ndi zina pamsika wa Salaula.

Chodabwitsa chinali chakuti, atafika pogula feteleza anadabwa poona kuti ndalama zomwe anasunga pa chitenje panalibe, malo mwake panapezeka mapepala amkaka wotsegulidwa kale.

Pakumva za nkhaniyi, a Harry Mkandawire anagwidwa ndi chisoni moti anapempha anthu amene angawadziwe mayiwa ndi cholinga chakuti awathandize powapatsa ndalama zomwe amafuna agulire fetelezazo.

“Asakane mayiwa. Ndipanga zotheka kuti ndiapatse K18,000 yomwe amafuna kugulira fetelezayo. Sindimakondwa ndikamaona azimayi akulira. Ndikhala ndili konko kumapeto kwa sabatayi, “ anatero a Mkandawire.

Cha ku m’mawaku, a Mkandawire anatuma anthu kuti akapereke thumba la feteleza komaso ndalama kwa mayiwa monga mwa lonjezo lawo.

Subscribe to our Youtube Channel:

Related Posts

LEAVE A REPLY

Please enter your comment!
Please enter your name here

Popular Articles