Monday, April 29, 2024

Featured Video

Latest Stories

Top 10 Music

Upcoming Events

Fact Up Night

Sat, 04 May 2024 20:00:00 UTC @ Club Casaulina - On 4th May 2024 Achina Gattah Ase and Gibo Pearson will be performing live for Fact Up Night at Club Casaulina in Lilongwe Area 25. The event will start from 8 PM till late More Info
Kapadocia Live In Mzuzu

Sun, 05 May 2024 13:00:00 UTC @ Rose Chanaichi's Gardens - Kapadocia will be performing live in Mzuzu Area 4 at Rose Chanaichi's Gardens on 05 May 2024. He will be supported by Rose Chanaichi Kayira, Motte Jez, Esther Mashani, Chipha Dada, Dele... More Info

Azibambo Anayi Amangidwa Atapezeka Ndi Ngaka Ya Moyo

Abambo anayi ali m’chitokosi cha polisi ya Lilongwe atapezeka akugulitsa Ngaka ya moyo ku Area 36 munzindawu.

Wachiwiri kwa mneneri wapolisi ya Lilongwe Khumbo Sanyiwa wati oganizilidwawa ndi a Stafford Omedi azaka 24, a Emmanuel Fabiano azaka azaka 30, a Paul Pelumbe azaka 41, a Bizwick Solomon azaka 40 komanso a Clement Juma wazaka 24.

Sanyiwa wati apolisi anakwanitsa kumanga abambowa atalandira uthenga kuchokera kwa anthu akufuna kwabwino kuti Omedi ndi Fabiano amagulitsa Ngaka yamoyo.

Ndipo apolisi anakwanitsa kumanga anthuwa pa malo ena omwesera mafuta pomwe anawapeza ndi nyamayi atayikutira musaka lomwe linayikidwa mu chikwama.

Sanyiwa wati awiriwa anatengeranso apolisi pamsika wa Kaphiri komwe anamanga anthu ena atatu omwe amayendesa nawo malondawa.

Oganizilidwawa akaonekera kubwalo la milandu posachedwapa kukayankha mlandu opezeka ndi Ngaka yamoyo opanda chilolezo.

Subscribe to our Youtube Channel:

Related Posts

Edgar Naitha
Edgar Naitha
Reporter|| Music Promotor|| Videographer Email: info@faceofmalawi.com

1 COMMENT

LEAVE A REPLY

Please enter your comment!
Please enter your name here

Popular Articles