Friday, May 3, 2024

Featured Video

Latest Stories

Top 10 Music

[showmfm]

Upcoming Events

[showevents]

Mwana Apha Bambo ake kamba Ka Mango

Apolisi mu m’zinda wa Blantyre amanga nyamata wa zaka 22 kamba adamenya bambo ake mpaka kuwapha pa nkhani ya Mango.

Potsimikizira nkhaniyi, M’neneri wa Polisi Sub Inspector Augustus Nkhwazi yemwe wanena kuti nyamatayi dzina lake ndi Arthur Maliro ndipo wapha bambo ake odziwika ndi dzina loti George Maliro ndipo adali ndi zaka 58.

Malingana ndi Nkhwazi, Pa 16 December, 2018 pa nthawi ya 11am, Arthur Maliro amathyola mango pafupi ndi nyumba ndipo bambo ake adauza Arthur kuti asiye kuthyola mangowo kamba kokuti mangowo sadaphye.

Ndipo izi zidakwiyitsa Arthur, kenako adatola botolo la galasi ndikuwagenda bambo ake m’mutu.

Bambo Maliro adakomoka pomwepo ndipo adathamangila nawo ku chipala cha Mpemba komwe madotolo adanena kuti bambo Maliro amwalira.

Bambo George Maliro amachokera m’mudzi mwa Nsomba T/A Nsomba mu mzinda wa Blantyre.

Sub Inspector Nkhwazi, wanena kuti Arthur Maliro atengeledwa ku Court pomwe apolisi ali kalikiliki kufufuza za nkhaniyi.

 

Related Posts

Face of Malawi
Face of Malawihttps://www.faceofmalawi.com
For more Info: info@faceofmalawi.com

LEAVE A REPLY

Please enter your comment!
Please enter your name here

Popular Articles