Thursday, April 25, 2024

Featured Video

Latest Stories

Top 10 Music

Upcoming Events

Zomba City Festival

Fri, 26 Apr 2024 10:00:00 UTC @ Botanic Garden - 2024 Zomba City Festival is schedulled to take place on 26 to 28 April at Botanic Garden in Zomba This is a festival for all ages in the historic mountain city of Zomba. Celebrate Cultu... More Info
Queens Club Shut Down

Fri, 26 Apr 2024 19:00:00 UTC @ Queens Club - Queens Club Presents "Queens Club Shut Down" with music performances by Kelly Kay, Charisma, Teddy Makadi and Praise Umali. The show will take place at Queens Club in Mzuzu on 26 April... More Info

Ndili ndi Kuthekera Kotukula Dziko La Malawi – Muluzi

Mtsogoleri wa Chipani chotsutsa cha United Democratic Front (UDF), Atupele Muluzi wati iye ali ndi kuthekera konse kotukula dziko la Malawi.

Muluzi in the middle

Muluzi wayankhula izi lachitatu lapitali pa msonkhano waukulu omwe chipani chake chidapangaitsa ku Blantyre pokonzekera zisankho zomwe zili nkudzazi.

“Ndimakonda dziko la Malawi ndipo ndili ndi masomphenya osintha zinthu. Ndimakhulupilira kuti kusintha ndikotheka pokha pokha ife ayini ake titaikirapo chidwi,” atero a Muluzi.

A Muluzi anonjezera kunena kuti ulimi wa fodya siukubweresaso phindu lokwanira choncho dziko la Malawi langoyenera kupeza njira zina zobweretsera chuma.

Ena omwe anayankhula ku msonkhanowo ndi mtsogoleri wakale wa dziko lino Dr Bakili Muluzi omwe anati nthawi yatha tsopano kuti atsogoleri azipani azilimbana ndi ndale zokokanakokana.

Iwo anapereka chitsaonzo cha mkazi wa mtsogoleri wakale wadziko lino, Callista Mutharika omwe mbuyomu m’mawu awo adanena anthu ena ochita ndale kuti ndi matchona ati kamba koti adakhalitsa kwambiri m’maiko akutali.

Subscribe to our Youtube Channel:

Related Posts

LEAVE A REPLY

Please enter your comment!
Please enter your name here

Popular Articles