Tuesday, April 16, 2024

Featured Video

Latest Stories

Top 10 Music

Upcoming Events

Zomba City Festival

Fri, 26 Apr 2024 10:00:00 UTC @ Botanic Garden - 2024 Zomba City Festival is schedulled to take place on 26 to 28 April at Botanic Garden in Zomba This is a festival for all ages in the historic mountain city of Zomba. Celebrate Cultu... More Info
Njuchi Day

Sat, 27 Apr 2024 10:00:00 UTC @ New Village House (Kampala Manase) - Elinationa And No Limit Presents Njuchi Day Music show with Njuchi Zitatu. The show will take place at New Village House in Manase on 27 April 2024 and it will have music performances b... More Info

MCP Sidzatengaso Boma Ine Ndili Moyo – Mutharika

Mtsogoleri wa dziko lino, Peter Mutharika wanenetsa kuti chipani chotsutsa cha Malawi Congress Party (MCP) sichidzalamuliraso dziko lino iye adakali moyo.

a Mutharika anenetsa kuti a Chakwera ndi chipani chawo cha MCP sichidzalamulira Malawi iwo ali moyo

Poyankhula lachinayi pa wailesi youlutsira mawu ya boma ya MBC, a Mutharika ati chipani cha MCP chomwe mtsogoleri wake ndi Dr Lazarus Chakwera sichidzaununkhaso utsogoleri wa dziko lino ati poti ndi chipani cha anthu okupha.

“Pokhapokha ngati Mutharika ali moyo, sindidzaalora amene aja kuti atenge ulamuliro wa dziko lino kachiwiri. Chimene chija ndi chipani cha anthu okupha choncho sindingaalore kudzapambana pa zisankho zikudzazi, “atero a Mutharika.

Pakadali pano, chipani cha MCP sichinayankhulepo kanthu pa mawu amene a Muntharika ayankhulawa.

Malinga ndi kafukufuku, zikuonetsa kuti chipani chotsutsa cha MCP chayamba kuposedwa mphamvu ndi  United Transform Movement (UTM) yomwe mtsogoleri wake ndi Dr Saulos Chilima.

Poyankhula za UTM, a Mutharika ati  a Chilima azinzawo ku UTM akumapanga misonkhano ndi cholinga chongofuna kunyoza atsogoleri aakuluakulu ku chipani cholamula cha Democratic Progressive Party (DPP).

Subscribe to our Youtube Channel:

Related Posts

LEAVE A REPLY

Please enter your comment!
Please enter your name here

Popular Articles