Sunday, April 28, 2024

Featured Video

Latest Stories

Top 10 Music

Upcoming Events

Zomba City Festival

Fri, 26 Apr 2024 10:00:00 UTC @ Botanic Garden - 2024 Zomba City Festival is schedulled to take place on 26 to 28 April at Botanic Garden in Zomba This is a festival for all ages in the historic mountain city of Zomba. Celebrate Cultu... More Info
Zeze We Wanna Party

Sun, 28 Apr 2024 13:00:00 UTC @ Uptown Lodge (Andiamo) - Uptown Lodge in Balaka Andiamo brings Zeze Kingston on Zeze We Wanna Party music show on 28th April 2024. The event will take place at Uptwon Lodge (Andiamo) starting from 1PM till late... More Info

Amangidwa Kaamba Kogwililira Mwana Wa Choir

A polisi ku Lilongwe amanga Jonas Herbert wa zaka 37 kaamba komuganizira kuti wagwilira mwana yemwe ndi wa choir wa zaka 14.

Malingana ndi mneneli wa polisi ya Lingadzi a Cassim Manda ati mkuluyu ndi otsogolera choir ya pa mpingo wina.

Iwo ati gululi linali ndi ulendo sabata yathayi opita kwa Njewa komwe adapita kukachita maimbidwe.

Kumeneku akuti makosanawa adapatsidwa malo ogona, atsikana kwa okha komanso anyamata kwa okha.

Koma a Manda ati anthu adadabwa kuona mkuluyu akukakamila m’chipinda mudali atsikana-mo kufikira kutada.

Iwo ati usiku mkuluyu adapezerapo mwayi ogwiragwira msungwanayu mpaka kukwanitsa kugona naye.

Apapatu ndi pomwe m’mawa wake asungwanawa adakafotokozera makosanawa a pa mpingo omwe adakauza a polisi za nkhaniyi.

Mkuluyu akuyembekezeka kukaonekera ku bwalo la milandu komwe akayankhe mlanduwu.

Herbert, amachokera ku Nathenje mfumu yaikulu Mazengera m’boma la Lilongwe.

Subscribe to our Youtube Channel:

Related Posts

Edgar Naitha
Edgar Naitha
Reporter|| Music Promotor|| Videographer Email: info@faceofmalawi.com

LEAVE A REPLY

Please enter your comment!
Please enter your name here

Popular Articles